32. nanena naye bwino, naika mpando wace upose mipando ya mafumu amene anali naye m'Babulo.
33. Ndipo anapindula zobvala zace za m'ndende, ndipo sanaleka kudya pamaso pace masiku onse a moyo wace.
34. Koma phoso lace mfumu ya ku Babulo sanaleka kumpatsa, phoso tsiku ndi tsiku gawo lace, mpaka tsiku la kufa kwace, masiku onse a moyo wace.