Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 49:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pakuti ndambvula Esau, ndambvundukula, sadzatha kubisala; mbeu zace zaonongeka, ndi abale ace, ndi anansi ace, ndipo palibe iye.

11. Siya ana ako amasiye, Ine ndidzawasunga; akazi ako amasiye andikhulupirire Ine.

12. Pakuti Yehova atero: Taonani, iwo amene sanaweruzidwa kuti amwe cikho adzamwadi; kodi iwe ndiye amene adzakhala wosalangidwa konse? sudzakhala wosalangidwa, koma udzamwadi.

13. Pakuti ndalumbira, Pali Ine, ati Yehova, kuti Boma adzakhala cizizwitso, citonzo, copasuka, ndi citemberero; ndipo midzi yace yonse idzakhala yopasuka cipasukire.

14. Ndamva mthenga wa kwa Yehoya, ndipo mthenga watumidwa mwa amitundu, wakuti, Sonkhanani, mumdzere, nimuukire nkhondo.

15. Pakuti, caona, ndakuyesa iwe wamng'ono mwa amitundu, ndi wonyozedwa mwa anthu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 49