Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:40-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Pakuti Yehova atero: Taonani, adzauluka ngati ciombankhanga, adzamtambasulira Moabu mapiko ace.

41. Keroti walandidwa, ndi malinga agwidwa, ndipo tsiku lomwelo mtima wa anthu amphamvu a Moabu adzakhala ngati mtima wa mkazi alinkudwala.

42. Ndipo Moabu adzaonongeka asakhalenso mtundu wa anthu, cifukwa anadzikuzira yekha pa Yehova.

43. Mantha, ndi dzenje, ndi khwekhwe, ziri pa iwe, wokhala m'Moabu, ati Yehova.

44. Ndipo iye wakuthawa cifukwa ca mantha adzagwa m'dzenje; ndi iye amene aturuka m'dzenje adzagwidwa m'khwekhwe; pakuti ndidzatengera pa iye, pa Moabu, caka ca kulangidwa kwao, ati Yehova.

45. Iwo amene anathawa aima opanda mphamvu pansi pa mthunzi wa Hesiboni; pakuti moto waturuka m'Hesiboni, ndi malawi a moto m'kati mwa Sihoni, nadya ngondya ya Moabu, ndi pakati pamtu pa ana a phokoso,

46. Tsoka iwe, Moabu! anthu a Kemosi athedwa; pakuti ana ako amuna atengedwa ndende, ndi ana ako akazi atengedwa ndende.

47. Koma ndidzabwezanso undende wa Moabu masiku akumariza, ati Yehova. Ziweruzo za Moabu ndi zomwezi.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48