Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:36-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Cifukwa cace mtima wanga umlima Moabu monga zitolilo, ndipo mtima wanga uwalirira anthu a Kireresi monga zitolilo, cifukwa cace zakucuruka zace adadzionera zatayika.

37. Pakuti mitu yonse iri yadazi, ndipo ndebvu ziri zosengedwa; pa manja onse pali pocekedwa-cekedwa, ndi pacuuno ciguduli.

38. Pamwamba pa macindwi a Moabu ndi m'miseu mwace muli kulira monse monse; pakuti ndaswa Moabu monga mbiya m'mene mulibe cikondwero, ati Yehova.

39. Yasweka bwanji! Akuwa bwanji Moabu! Wapotoloka bwanji ndi manyazi! Comweco Moabu adzakhala coseketsa ndi coopsera onse omzungulira iye.

40. Pakuti Yehova atero: Taonani, adzauluka ngati ciombankhanga, adzamtambasulira Moabu mapiko ace.

41. Keroti walandidwa, ndi malinga agwidwa, ndipo tsiku lomwelo mtima wa anthu amphamvu a Moabu adzakhala ngati mtima wa mkazi alinkudwala.

42. Ndipo Moabu adzaonongeka asakhalenso mtundu wa anthu, cifukwa anadzikuzira yekha pa Yehova.

43. Mantha, ndi dzenje, ndi khwekhwe, ziri pa iwe, wokhala m'Moabu, ati Yehova.

44. Ndipo iye wakuthawa cifukwa ca mantha adzagwa m'dzenje; ndi iye amene aturuka m'dzenje adzagwidwa m'khwekhwe; pakuti ndidzatengera pa iye, pa Moabu, caka ca kulangidwa kwao, ati Yehova.

45. Iwo amene anathawa aima opanda mphamvu pansi pa mthunzi wa Hesiboni; pakuti moto waturuka m'Hesiboni, ndi malawi a moto m'kati mwa Sihoni, nadya ngondya ya Moabu, ndi pakati pamtu pa ana a phokoso,

46. Tsoka iwe, Moabu! anthu a Kemosi athedwa; pakuti ana ako amuna atengedwa ndende, ndi ana ako akazi atengedwa ndende.

47. Koma ndidzabwezanso undende wa Moabu masiku akumariza, ati Yehova. Ziweruzo za Moabu ndi zomwezi.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48