Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Za Moabu Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Tsoka Nebo! pakuti wapasuka; Kiriyataimu wacitidwa manyazi, wagwidwa; linga la pamtunda lacitidwa manyazi lapasudwa.

2. Palibenso kutamanda Moabu; m'Hesiboni anamlingiririra zoipa, ndi kuti, Tiyeni, tiwathe asakhalenso mtundu waanthu. Iwenso, Madimeni, udzatontholetsedwa, lupanga lidzakulondola iwe.

3. Mau amveka kucokera ku Horonaimu, kufunkha ndi kuononga kwakukuru!

4. Moabu waonongedwa; ang'ono ace amveketsa kulira.

5. Pakuti adzakwera pa cikweza ca Luhiti ndi kulira kosaleka; pakuti pa citsiko ca Horonaimu amva kulira kowawa kwa cionongeko.

6. Thawani, pulumutsani miyoyo yanu, mukhale amarisece m'cipululu,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48