3. Pomveka migugu ya ziboda za olimba ane, pogumukira magareta ace, ndi pophokosera njinga zace, atate sadzaceukira ana ao cifukwa ca kulefuka kwa manja ao;
4. cifukwa ca tsiku lakudzafunkha Afilisti onse, kuphera Turo ndi Zidoni othangata onse akutsala; pakuti Yehova adzafunkha Afilisti, otsala a cisumbu ca Kafitori.
5. Dazi lafikira a Gaza; Asikeloni wathedwa, otsala m'cidikha cao; udzadziceka masiku angati?
6. Iwe lupanga la Yehova, atsala masiku angati osakhala cete iwe? dzilonge wekha m'banzi lako; puma, nukhale cete.
7. Udzakhala cete bwanji, popeza Yehova anakulangiza? za Asikeloni, ndi za m'mbali mwa nyanja, pamenepo analiika.