Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 46:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mangani akavalo, bwerani, inu apakavalo, imani ndi zisoti zacitsulo; tuulani nthungo zanu, bvalani malaya acitsulo.

5. Cifukwa canji ndaciona? aopa, abwerera; amphamvu ao agwetsedwa, athawadi, osaceukira m'mbuyo; mantha ali ponseponse, ati Yehova.

6. Waliwiro asathawe, wamphamvu asapulumuke; kumpoto pambali pa nyanja ya Firate wapunthwa nagwa.

7. Ndani uyu amene auka ngati Nile, madzi ace ogabvira monga nyanja?

8. Aigupto auka ngati Nile, madzi ace agabvira ngati nyanja; ndipo ati, Ndidzauka, ndidzamiza dziko lapansi; ndidzaononga mudzi ndi okhalamo ace.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 46