Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 46:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mau a Yehova amene anadza kwa Yeremiya mneneri akunena za amitundu.

2. Za Aigupto: kunena za nkhondo ya Farao-neko mfumu ya Aigupto, imene inali pa nyanja ya Firate m'Karikemisi, imene anaikantha Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo caka cacinai ca Yehoyakimu mwana wace wa Yosiya, mfumu ya Yuda.

3. Konzani cikopa ndi lihawo, nimuyandikire kunkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 46