Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 43:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali pamene Yeremiya anatha kunena kwa anthu onse mau onse a Yehova Mulungu wao, amene anamtuma iye nao Yehova Mulungu wao, mau onse amenewo,

2. pamenepo ananena Azariya mwana wace wa Hosaya, ndi Yohanani mwana wace wa Kareya, ndi anthu onse odzikuza, nati kwa Yeremiya, Unena zonama; Yehova Mulungu wathu sanakutumiza iwe kudzanena, Musalowe m'Aigupto kukhala m'menemo;

3. koma Baruki mwana wace wa Neriya aticicizira inu, mutipereke m'dzanja la Akasidi, kuti atiphe ife, atitengere ife am'nsinga ku Babulo.

4. Ndipo Yohanani mwana wace wa Kareya, ndi akazembe onse a nkhondo, ndi anthu onse sanamvera mau a Yehova, kuti akhale m'dziko la Yuda.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 43