Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 42:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma mukati, Sitidzakhala m'dziko muno; osamvera mau a Yehova Mulungu wanu;

14. ndi kuti, Iai; tidzanka ku Aigupto, kumene sitidzaona nkhondo, sitidzamva kulira kwa lipenga, sitidzamva njala yokhumba mkate; pamenepo tidzakhala;

15. cifukwa cace mumve mau a Yehova, Otsala inu a Yuda, atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, Ngati mulozetsa nkhope zanu kuti mulowe m'Aigupto, kukakhala m'menemo;

16. pamenepo padzakhala, kuti lupanga limene muopa lidzakupezani m'menemo m'dziko la Aigupto, ndi njala, imene muiopa, idzakuumirirani kumeneko ku Aigupto; pamenepo mudzafa.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 42