Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 4:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Pakuti anthu anga apusa, sandidziwa Ine; ali ana opulukira sazindikira; ali ocenjera kucita coipa koma kucita cabwino sakudziwa.

23. Ndinaona dziko lapansi, ndi rpo taona, linali lopasuka lopanda kanthu; ndipo ndinaona kumwamba, kunalibe kuunika.

24. Ndinaona mapiri, taona ananthunthumira; ndipo zitunda zonse zinagwedezeka.

25. Ndinaona, ndipo taona, panalibe munthu, ndi mbalame zonse zakumwamba zinathawa.

26. Ndinaona, ndipo taona, munda wazipatso unali cipululu, ndipo midzi yace yonse inapasuka pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa mkwiyo wace woopsya.

27. Pakuti Yehova atero, Dziko lonse lidzakhala bwinja koma sindidzatsirizitsa.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 4