Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 38:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo pamene Ebedi-Meleki Mkusi, mdindo, anamva kuti anamuika Yeremiya m'dzenje; mfumu irikukhala pa cipata ca Benjamini;

8. Ebedi-Meleki anaturuka m'nyumba ya mfumu, nanena ndi mfumu, kuti,

9. Mbuyanga mfumu, anthu awa anacita zoipa m'zonse anacitira Yeremiya mneneri, amene anamponya m'dzenje; ndipo afuna kufa m'menemo cifukwa ca njala; pakuti mulibe cakudya cina m'mudzimu.

10. Ndipo mfumu inamuuza Ebedi-Meleki Mkusi, kuti, Tenga anthu makumi atatu, umkweze numturutse Yeremiya mneneri m'dzenjemo, asanafe.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 38