Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 37:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli: Muzitero kwa mfumu ya Yuda, imene inakutumani inu kwa Ine kuti mundifunse Ine: Taonani, nkhondo ya Farao, yakuturukira kudzathandiza inu, idzabwerera ku Aigupto ku dziko lao.

8. Ndipo Akasidi adzabweranso, nadzamenyana ndi mudzi uwu; ndipo adzaulanda, nadzautentha ndi moto.

9. Yehova atero: Musadzinyenge, kuti, Akasidi adzaticokera ndithu; pakuti sadzacoka.

10. Pakuti ngakhale mukadakantha nkhondo yonse ya Akasidi akumenyana, nanu, ngakhale akadatsala olasidwa okha okha mwa iwo, koma iwowa akadauka yense m'hema wace ndi kutentha mudzi uwu ndi moto.

11. Ndipo panali pamene nkhondo ya Akasidi inacoka ku Yerusalemu cifukwa ca nkhondo ya Farao,

12. pamenepo Yeremiya anaturuka m'Yerusalemu kumuka ku dziko la Benjamini, kukalandira gawo lace kumeneko.

13. Pokhala iye m'cipinda ca Benjamini, kapitao wa alonda anali kumeneko, dzina lace Iriya, mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya; ndipo iye anamgwira Yeremiya mneneri, nati, Ulinkupandukira kwa Akasidi.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 37