Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 37:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pokhala iye m'cipinda ca Benjamini, kapitao wa alonda anali kumeneko, dzina lace Iriya, mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya; ndipo iye anamgwira Yeremiya mneneri, nati, Ulinkupandukira kwa Akasidi.

14. Ndipo anati Yeremiya, Kunama kumeneko; ine sindipandukira kwa Akasidi; koma sanamvera iye; ndipo Iriya anamgwira Yeremiya, nanka naye kwa akuru.

15. Ndipo akuru anakwiyira Yeremiya, nampanda iye, namuika m'nyumba yandende m'nyumba ya Yonatani mlembi; pakuti anaiyesa ndende.

16. Atafika Yeremiya ku nyumba yadzenje, ku tizipinda tace nakhalako Yeremiya masiku ambiri;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 37