Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 34:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. cifukwa cace mau a Yehova anadza kwa Yeremiya kucokera kwa Yehova, kuti,

13. Yehova Mulungu wa Israyeli atero: Ndinapangana mapangano ndi makolo anu tsiku lija ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto, kuturuka m'nyumba ya ukapolo, kuti,

14. Zitapita zaka zisanu ndi ziwiri mudzaleka amuke yense mbale wace amene ali Mhebri, amene anagulidwa ndi inu, amene anakutumikirani inu zaka zisanu ndi cimodzi, mudzammasule akucokereni; koma makolo anu sanandimvera Ine, sanandichera Ine khutu,

15. Ndipo mwabwerera inu tsopano, ndi kucita cimene ciri colungama pamaso panga, pakulalikira ufulu yense kwa mnzace; ndipo munapangana pangano pamaso panga m'nyumba imene ichedwa dzina langa;

16. koma mwabwerera ndi kuipitsa dzina langa, ndi kubwezera m'ukapolo yense kapolo wace wamwamuna, ndi wamkazi, amene munammasula akacite zao, ndipo munawagonjetsa, akhale akapolo anu amuna ndi akazi.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 34