Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 33:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya, kuti,

24. Kodi sulingalira comwe anena anthu awa, kuti, Mabanja awiri amene Yehova anawasankha, wataya iwo? comweco anyoza anthu anga, kuti asakhalenso mtundu pamaso pao.

25. Yehova atero: Likaleka kukhala pangano langa la usana ndi usiku, ngati sindinalemba malemba a kumwamba ndi dziko lapansi;

26. pamenepo ndidzatayanso mbeu ya Yakobo, ndi ya Davide mtumiki wanga, kuti sindidzatenganso za mbeu zace kuti zikhale zolamulira mbeu za Abrahamu, ndi za Isake, ndi za Yakobo; pakuti ndidzabweundende wao, ndipo ndidzawacitira cifundo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 33