Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 32:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo ndinatenga kalata wogulira, wina wosindikizidwa, monga mwa lamulo ndi mwambo, ndi wina wobvundukuka;

12. ndipo ndinapereka kalata wogulirayo kwa Baruki mwana wa Neriya, mwana wa Maseya, pamaso pa Hanameli mwana wa mbale wa atate wanga, ndi pamaso pa mboni zimene zinalemba pa kalata wogulirayo, pamaso pa Ayuda onse okhala m'bwalo la kaidi.

13. Ndipo ndinauza Baruki pamaso pao, kuti,

14. Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero; Tenga akalata awa, kalata uyu wogulira, wosindikizidwa, ndi kalata uyu wobvundukuka, nuwaike m'mbiya yadothi; kuti akhale masiku ambiri.

15. Pakuti Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero: Nyumba ndi minda ndi minda yamphesa idzagulidwanso m'dziko muno.

16. Ndipo nditapereka kalata wogulirayo kwa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova, kuti,

17. Ha! Yehova Mulungu, taonani, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi mphamvu yanu yaikuru ndi mkono wanu wotambasuka; palibe cokulakani Inu;

18. a amene mucitira cifundo anthu zikwi; nimubwezera mphulupulu ya atate m'cifuwa ca ana ao a pambuyo pao, dzina lace ndi Mulungu wamkuru, wamphamvu, Yehova wa makamu;

19. wamkuru, m'upo, wamphamvu m'nchito; maso anu ali otsegukira njira zonse za ana a anthu; kuti mupatse yense monga mwa cipatso ca macitidwe ace;

20. amene munaika zizindikiro ndi zodabwitsa m'dziko la Aigupto, mpaka lero lomwe, m'Israyeli ndi mwa anthu ena; nimunadzitengera mbiri, monga lero lomwe;

21. ndipo munaturutsa anthu anu Israyeli m'dziko la Aigupto ndi zizindikiro, ndi zodabwitsa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi mantha ambiri;

22. ndipo munawapatsa iwo dziko ili, limene munalumbirira makolo ao kuti mudzawapatsa, dziko moyenda mkaka ndi uci;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 32