Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 31:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo Yuda ndi midzi yace yonse adzakhalamo pamodzi; alimi, ndi okusa zoweta.

25. Pakuti ndakhutidwa mtima wolema, ndadzazanso mtima uli wonse wacisoni.

26. Pamenepo ndinauka, ndinaona; ndipo tulo tanga tinandizunira ine.

27. Taonani, masiku adza, ati Yehova, amene ndidzafesera nyumba ya Israyeli ndi nyumba ya Yuda ndi mbeu ya anthu ndi mbeu ya nyama.

28. Ndipo padzakhala kuti, monga ndayang'anira iwo kuzula ndi kupasula ndi kugwetsa, ndi kuononga ndi kusautsa; momwemo ndidzayang'anira iwo kumangitsa mudzi ndi kubzyala, ati Yehova.

29. Masiku omwewo sadzanenanso, Atate adya mphesa zowawa, ndi mano a ana ayayamira.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 31