1. Mau amene anadza kwa Yeremiya kucokera kwa Yehova, kuti,
2. Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, kuti, Lemba m'buku mau onse amene ndanena kwa iwe.
3. Pakuti, taona, masiku adzadza, ati Yehova, amene ndidzabwezanso undende wa anthu anga Aisrayeli ndi Ayuda, ati Yehova; ndipo ndidzawabwezera ku dziko limene ndinapatsa makolo ao. Ndipo adzakhala nalo.
4. Awa ndi mau ananena Yehova za Israyeli ndi Yuda.