Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 3:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Bwerani, ana inu obwerera, ndidzaciritsa mabwerero anu. Taonani, tadza kwa Inu; pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.

23. Ndithu akhulupirira mwacabe cithandizo ca kuzitunda, ndi phokoso la kumapiri; ndithu mwa Yehova Mulungu wathu muli cipulumutso ca Israyeli,

24. Ndipo cocititsa manyazi cinathetsa nchito za atate athu kuyambira ubwana wathu; nkhosa zao ndi zoweta zao, ana ao amuna ndi akazi.

25. Tigone m'manyazi athu, kunyala kwathu kutipfunde ife; pakuti tamcimwira Yehova Mulungu wathu, ife ndi makolo athu, kuyambira ubwana wathu kufikira lero lomwe; ndipo sitidamvera mau a Yehova Mulunguwathu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 3