Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 29:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Pamenepo mudzandiitana Ine, ndipo mudzanka ndi kupemphera kwa Ine, ndipo ndidzakumverani inu.

13. Ndipo mudzandifuna Ine, ndi kundipeza, pamene mundifuna ndi mtima wanu wonse.

14. Ndipo ndidzapezedwa ndi inu, ati Yehova, ndidzabwezanso undende wanu, ndipo ndidzasonkhanitsa inu kwa mitundu yonse, ndi kumalo konse kumene ndinakupitikitsirani inu, ati Yehova; ndipo ndidzakubwezeraninso kumalo kumene ndinakutengani inu andende.

15. Pakuti mwati, Yehova watiutsira ife aneneri m'Babulo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 29