Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 27:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. nuzitumize kwa mfumu ya Edomu, ndi kwa mfumu ya Moabu, ndi kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kwa mfumu ya Turo, ndi kwa mfumu ya Zidoni, ndi dzanja la amithenga amene afika ku Yerusalemu kwa Zedekiya mfumu ya Yuda;

4. nuwauze iwo anene kwa ambuyao, kuti, Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero: Muzitero kwa ambuyanu:

5. Ine ndinalenga dziko lapansi, anthu ndi nyama zokhala m'dzikomo, ndi mphamvu yanga yaikuru ndi mkono wanga wotambasuka; ndipo ndinapereka ilo kwa iye amene ayenera pamaso panga.

6. Tsopano ndapereka maiko onse awa m'manja a Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo, mtumiki wanga; ndiponso nyama za kuthengo ndampatsa iye kuti zimtumikire.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 27