Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 26:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. ndipo pamene Yehoyakimu mfumu, ndi amphamvu ace onse, ndi akuru onse, anamva mau ace, mfumu inafuna kumupha iye; koma pamene Uriya anamva, anaopa, nathawa, nanka ku Aigupto;

22. ndipo Yehoyakimu mfumu anatuma anthu ku Aigupto, Elinatanu mwana wace wa Akibori, ndi anthu ena pamodzi ndi iye, anke ku Aigupto;

23. ndipo anamturutsa Uriya m'Aigupto, nanka naye kwa Yehoyakimu mfumu; amene anamupha ndi lupanga, naponya mtembo wace m'manda a anthu acabe.

24. Koma dzanja la Ahikamu mwana wa Safani linali ndi Yeremiya, kuti asampereke m'manja a anthu kuti amuphe.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 26