Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 25:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pakuti Yehova, Mulungu wa Israyeli, atero kwa ine, Tenga cikho ca vinyo wa ukaliwu pa dzanja langa, ndi kumwetsa mitundu yonse, imene ndikutumizirako.

16. Ndipo adzamwa, nadzayenda dzandi dzandi, nadzacita misala, cifukwa ca lupanga limene Ine ndidzatumiza mwa iwo.

17. Ndipo ndinatenga cikho pa dzanja la Yehova, ndinamwetsa mitundu yonse, imene Yehova ananditumizirako;

18. Yerusalemu, ndi midzi ya Yuda, ndi mafumu ace omwe, ndi akuru ace, kuwayesa iwo bwinja, cizizwitso, cotsonyetsa, ndi citemberero; monga lero lino;

19. Farao mfumu ya ku Aigupto, ndi atumiki ace, ndi akuru ace, ndi anthu ace onse;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 25