Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 22:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Cifukwa cace Yehova atero za Yehoyakimu mwana wace wa Yosiya, mfumu ya Yuda: Sadzamlira iye, kuti, Kalanga ine mbale wanga! kapena, Kalanga ine mlongo wanga! Sadzamlira, kuti, Kalanga ine mbuye! kapena, Kalanga ine ulemerero wace!

19. Adzamuika monga kuika buru, adzamkoka nadzamponya kunja kwa zipata za Yerusalemu.

20. Kwera ku Lebano, nupfuule; kweza mau ako m'Basani; nupfuule m'Abarimu; pakuti mabwenzi ako onse atha,

21. Ndinanena ndi iwe m'phindu lako; koma unati, Sindidzamva. Awa ndi makhalidwe ako kuyambira ubwana wako, kuti sudamvera mau anga,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 22