Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 2:19-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Coipa cako cidzai kulanga iwe, mabwerero ako adzakudzudzula iwe; dziwa, nuone, kuti ici ndi coipa ndi cowawa, kuti wasiya Yehova Mulungu wako, ndi kuti kundiopa Ine sikuli mwa iwe, ati Yehova Mulungu wa makamu.

20. Pakuti kale lomwe ndinatyola gori lako, ndi kudula zomangira zako; ndipo unati, Sindidzakutumikirani, pakuti pa zitunda zonse zazitari, ndi patsinde pa mitengo yonse yaiwisi unawerama, ndi kucita dama.

21. Ndipo Ine ndinakuoka mpesa wangwiro, mbeu yoona; kodi bwanji wandisandukira Ine mbeu yopanda pace, ya mpesa wacilendo?

22. Pakuti ngakhale usamba ndi soda, ndi kudzitengera sopo wambiri, mphulupulu zako zidziwika pamaso panga, ati Yehova Mulungu.

23. Bwanji uti, Sindinaipitsidwa, sindinatsata Abaala? Ona njira yako m'cigwa, dziwa cimene wacicita; ndiwe ngamila yothamanga yoyenda m'njira zace;

24. mbidzi yozolowera m'cipululu, yopumira mphepo pakufuna pace; pokomana nayo ndani adzaibweza? onse amene aifuna sadzadzilemetsa; adzaipeza m'mwezi wace.

25. Kaniza phazi lako lisakhale losabvala nsapato, ndi m'mero mwako musakhale ndi ludzu; koma unati, Palibe ciyembekezo, iai; pakuti ndakonda alendo, ndipo ndidzatsata pambuyo pao.

26. Monga mbala iri ndi manyazi pamene igwidwa, comweco nyumba ya Israyeli iri ndi manyazi; iwo, mafumu ao, akuru ao, ansembe ao, ndi aneneri ao;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 2