Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 19:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndidzatero ndi malo ano, ati Yehova, ndi okhalamo, kusanduliza mudzi uwu ngati Tofeti;

13. ndi nyumba za Yerusalemu, ndi nyumba za mafumu a Yuda, zimene ziipitsidwa, zidzanga malo a Tofeti, ndizo nyumba zonse anafukizira khamu lonse la kumwamba pa matsindwi ao, ndi kuithirira milungu yina nsembe zothira.

14. Pamenepo Yeremiya anadza kucokera ku Tofeti, kumene Yehova anamtuma iye kuti anenere; ndipo anaima m'bwalo la nyumba ya Yehova, nati kwa anthu onse:

15. Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero, Taonani, ndidzatengera mudzi uwu ndi midzi yace yonse coipa conse cimene ndaunenera; cifukwa anaumitsa khosi lao, kuti asamve mau anga.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 19