Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 17:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cimo la Yuda lalembedwa ndi peni lacitsulo, ndi nsonga ya diamondi; lalembedwa pa colembapo ca m'mtima mwao, ndi pa nyanga za maguwa a nsembe anu.

2. Pokumbukira ana ao maguwa a nsembe ao ndi zoimiritsa zao ku mitengo yaiwisi ya pa zitunda zazitari.

3. Iwe phiri langa la m'munda, ndidzapereka cuma cako ndi zosungidwa zako zikafunkhidwe, ndi misanje yako, cifukwa ca cimo, m'malire ako onse.

4. Iwe, iwe wekha, udzaleka pa colowa cako cimene ndinakupatsa iwe; ndipo ndidzakutumikiritsa adani ako m'dziko limene sulidziwa; pakuti wakoleza moto m'mkwiyo wanga umene udzatentha ku nthawi zamuyaya.

5. Atero Yehova: Wotembereredwa munthu amene akhulupirira munthu, natama mkono wanyama, nucoka kwa Yehova mtima wace.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 17