Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 16:19-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Inu Yehova, mphamvu yanga, ndi linga langa, pothawirapo panga tsiku la msauko, amitundu adzadza kwa Inu kucokera ku malekezero a dziko lapansi, ndipo adzati, Makolo athu analandira colowa ca bodza lokha, zopanda pace ndi zinthu zosapindula nazo.

20. Kodi munthu adzadzipangira yekha milungu, imene siiri milungu?

21. Cifukwa cace, taonani, ndidzadziwitsa iwo kamodzi aka, ndidzawadziwitsa dzanja langa ndi mphamvu yanga; ndipo adzadziwa kuti dzina langa ndine Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 16