Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 16:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Poyamba ndibwezera mphulupulu yao ndi cimo lao cowirikiza; cifukwa anaipitsa dziko langa ndi mitembo ya zodetsedwa zao, nadzaza colowa canga ndi zonyansa zao.

19. Inu Yehova, mphamvu yanga, ndi linga langa, pothawirapo panga tsiku la msauko, amitundu adzadza kwa Inu kucokera ku malekezero a dziko lapansi, ndipo adzati, Makolo athu analandira colowa ca bodza lokha, zopanda pace ndi zinthu zosapindula nazo.

20. Kodi munthu adzadzipangira yekha milungu, imene siiri milungu?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 16