Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 15:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Kupweteka kwanga kuti cipwetekere bwanji, ndi bala langa losapoleka, likana kupola? kodi mudzakhala kwa ine ngati kamtsinje konyenga, ngati madzi omwerera?

19. Cifukwa cace atero Yehova, Ukabwerera pamenepo ndidzakubwezanso, kuti uime pamaso panga; ndipo ukasiyanitsa ca mtengo wace ndi conyansa, udzakhala ngati m'kamwa mwanga; ndipo adzabwerera kwa iwe, koma sudzabwerera kwa iwo.

20. Ndidzakuyesa iwe linga lamkuwa la anthu awa; ndipe adzamenyana ndi iwe, koma iwo sadzakuposa iwe; pakuti Ine ndiri ndi iwe kuti ndikupulumutse ndi kukulanditsa iwe, ati Yehova.

21. Ndipo ndidzakulanditsa iwe m'dzanja la oipa, ndipo ndidzakuombola iwe m'dzanja la oopsya.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 15