Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mau a Yehova amene anadza kwa Yeremiya onena za cirala.

2. Yuda alira, ndipo zipata zace zilefuka, zikhala pansi zobvekedwa ndi zakuda; mpfuu wa Yerusalemu wakwera.

3. Akuru ao atuma ang'ono ao kumadzi; afika kumaenje, osapeza madzi; abwera ndi mitsuko yao yopanda kanthu; ali ndi manyazi, athedwa nzeru, apfunda mitu yao.

4. Cifukwa ca nthaka yocita ming'aru, pakuti panalibe mvula padziko, olima ali ndi manyazi, apfunda mitu yao.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 14