Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 13:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Koma ngati simudzamva, moyo wanga udzalira m'tseri cifukwa ca kunyada kwanu; diso langa lidzalira kwambiri, lidzagwa misozi, cifukwa zoweta za Yehova zagwidwa m'nsinga.

18. Nenani kwa mfumu ndi kwa amace wa mfumu, Dzicepetseni, khalani pansi; pakuti zapamtu zanu zagwa, korona wanu wokoma.

19. Midzi ya ku Mwera yatsekedwa, palibe wotsegulira. Yuda wonse wacotsedwa m'ndende wonsewo, wacotsedwa m'nsinga.

20. Tukulani maso anu, taonani iwo amene acokera kumpoto; ziri kuti zoweta zinapatsidwa kwa iwe, zoweta zako zokoma?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 13