Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 11:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma ine ndinanga mwana wa nkhosa wofatsa wotengedwa kukaphedwa; ndipo sindinadziwa kuti anandicitira ine ciwembu, kuti, Tiononge mtengo ndi zipatso zace, timdule iye pa dziko la amoyo, kuti dzina lace lisakumbukikenso.

20. Koma, Yehova wa makamu, amene aweruza molungama, pamene ayesa imso ndi mtima, ndikuoneni Inu mulikuwabwezera cilango, pakuti kwa Inu ndaulula mlandu wanga.

21. Cifukwa cace atero Yehova za anthu a Anatoti, amene afuna moyo wanga, kuti, Usanenere m'dzina la Yehova, ungafe ndi mkono wathu;

22. cifukwa cace atero Yehova wa makamu, Taonani, ndidzalanga iwo; anyamata adzafa ndi lupanga; ana ao amuna ndi akazi adzafa ndi njala;

23. ndipo sadzakhala nao otsalira; pakuti ndidzatengera coipa pa anthu a ku Anatoti, caka ca kulangidwa kwao.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 11