Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 2:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo taona, Boazi anafuma ku Betelehemu, nati kwa oceka, Yehova akhale nanu. Namyankha iwo, Yehova akudalitseni.

5. Nati Boazi kwa mnyamata wace woyang'anira ocekawo, Mkazi uyu ngwa yani?

6. Ndipo mnyamata woyang'anira ocekawo anayankha nati, Ndiye mkazi Mmoabuyo anabwera ndi Naomi ku dziko la Moabu;

7. ndipo anati, Undilole, ndikunkhe ndiole pakati pa mitolo potsata ocekawo; nadza iye nakhalakhala kuyambira m'mawa mpaka tsopano; koma m'nyumba samakhalitsamo.

8. Pamenepo Boazi ananena ndi Rute, Ulikumva, mwana wanga? Usakakunkha m'munda mwina, kapena kupitirira pano, koma uumirire adzakazi anga mommuno.

9. Maso ako akhale pa munda acekawo, ndi kuwatsata; kodi sindinawauza anyamata asakukhudze? Ndipo ukamva ludzu, muka kumitsuko, ukamweko otunga anyamatawo,

10. Potero anagwa nkhope yace pansi, nadziweramira pansi, nanena naye, Mwandikomera mtima cifukwa ninji kuti mundisamalira ine, popeza ndine mlendo?

Werengani mutu wathunthu Rute 2