Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 2:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Nati Rute Mmoabu kwa Naomi, Mundilole ndimuke kumunda, ndikatole khunkha is ngala za tirigu, kumtsata iye amene adzandikomeramtima. Nanena naye, Muka, mwana wanga.

3. Namuka iye, nakatola khunkha m'munda namatsata ocekawo; ndipo kudangotero naye kuti deralo la munda linali la Boazi, ndiye wa banja la Elimeleki.

4. Ndipo taona, Boazi anafuma ku Betelehemu, nati kwa oceka, Yehova akhale nanu. Namyankha iwo, Yehova akudalitseni.

5. Nati Boazi kwa mnyamata wace woyang'anira ocekawo, Mkazi uyu ngwa yani?

Werengani mutu wathunthu Rute 2