Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 1:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.

11. Nati Naomi, Bwererani, ana anga, mudzatsagana nane bwanji? ngati ndiri nao m'mimba mwanga ana amuna ena kuti akhale amuna anu?

12. Bwererani, ana anga, mukani, pakuti ndakalambitsa ine, sindikhoza kukhala naye mwamuna. Ngakhale ndikati, Ndiri naco ciyembekezo, ndikakhala naye mwamuna usiku uno, ndi kubalanso ana amuna;

13. kodi mudzawalindirira akakula? mudzadziletsa osakwatibwa? Iai, ana anga, pakuti candiwawa koposa cifukwa ca inu popeza dzanja la Yehova landiturukira.

14. Nakweza iwo mau ao, naliranso misozi; ndi Olipa anampsompsona mpongozi wace, koma Rute anamkangamira.

15. Pamenepo anati, Taona mbale wako wabwerera kwa anthu a kwao, ndi kwa mulungu wace, bwerera umtsate mbale wako.

16. Nati Rute, Musandiumirize kuti ndikusiyeni, ndi kubwerera osakutsatani; pakuti kumene mumukako ndimuka inenso, ndi kumene mugonako ndigona inenso; anthu a kwanu ndiwo anthu a kwa inenso, ndi Mulungu wanu ndiye Mulungu wanga;

17. kumene mudzafera inu ine ndidzafera komweko, ndi kuikidwa komweko; andilange Yehova naonjezeko, ciri conse cikasiyanitsa inu ndi ine, koma imfa ndiyo.

Werengani mutu wathunthu Rute 1