Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 9:52-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

52. Ndipo Abimeleki anafika kunsania, nalimbana nayo nkhondo, nayandikira kukhomo kwa nsanja, aitenthe ndi moto.

53. Ndipo mkazi wina anaponya mwana wa mphero pamutu pa Abimeleki, naphwanya bade lace.

54. Pamenepo anaitana msanga mnyamata wace wosenza zida zace, nanena naye, Solola lupanga lako nundiphe, angamanenere anthu, ndi kuti, Anamupha ndi mkazi. Nampyoza mnyamata wace, nafa iye.

55. Pamene amuna a Israyeli anaona kuti adafa Abimeleki anamuka yense kumalo kwace.

56. Momwemo Mulungu anambwezera Abimeleki coipaco anacitira atate wace ndi kuwapha abale ace makumi asanu ndi awiri.

57. Ndipo Mulungu anawabwezera coipa conse ca amuna a ku Sekemu pamitu pao, ndipo linawagwera temberero la Yotamu mwana wa Yerubaala.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 9