Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 9:46-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Ndipo pamene eni ace onse a nsanja ya ku Sekemu anacimva, analowa m'ngaka ya nyumba ya Eliberiti.

47. Ndipo anauza Abimeleki kuti amuna onse a nsanja ya ku Sekemu asonkhane.

48. Pamenepo Abimeleki anakwera kumka ku phiri la Zalimoni, iye ndi anthu onse anali naye; natenga nkhwangwa m'dzanja lace Abimeleki, nadula nthambi kumitengo, nainyamula ndi kulika paphewa pace, nati kwa anthu okhala naye, Ici munaciona ndacita, fulumirani, mucite momwemo.

49. Ndi anthu onse anadulanso yense nthambi yace, natsata Abimeleki, naziika pangaka, natentha nazo ngakayo ndi moto; motero anthu onse a nsanja ya ku Sekemu anafanso, amuna ndi akazi ngati cikwi cimodzi.

50. Pamenepo Abimeleki anamuka ku Tebetsi, naumangira Tebetsi misasa, naulanda.

51. Koma m'mudzimo munali nsanja yolimba nathawira kumeneko amuna ndi akazi onse, ndi eni ace onse a mudziwo, nadzitsekereza m'mwemo, nakwera patsindwi pa nsanja.

52. Ndipo Abimeleki anafika kunsania, nalimbana nayo nkhondo, nayandikira kukhomo kwa nsanja, aitenthe ndi moto.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 9