Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 9:29-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Mwenzi anthu awa akadakhala m'dzanja langa; ndikadamcotsadi Abimeleki. Ndipo anati kwa Abimeleki, Curukitsa khamu lako, nuturuke.

30. Pamene Zebuli woyang'anira mudzi anamva mau a Gaala mwana wa Ebedi, anapsa mtima.

31. Natuma mithenga kwa Abimeleki monyenga nati, Taonani Gaala ndi abale ace afika ku Sekemu; ndipo taonani, akupandukitsirani mudzi.

32. Ndipo tsopano, taukani usiku, inu ndi anthu okhala nanu ndi kulalira kuthengo;

33. ndipo kukhale kuti m'mawa, pakuturuka dzuwa, muuke mamawa mugwere mudziwo; ndipo taonani, akakuturukirani iye ndi anthu ali naye, uzimcitira monga lidziwa dzanja lako.

34. Pamenepo Abimeleki anauka ndi anthu onse anali naye, usiku; nalalira a ku Sekemu, magulu anai.

35. Ndipo Gaala mwana wa Ebedi anaturuka, naima polowera pa cipata ca mudzi; nauka Abimeleki ndi anthu anali naye m'molalira.

36. Ndipo pamene Gaala anapenya anthuwo anati kwa Zebuli, Taona, alikutsika anthu kucokera pamwamba pa mapiri, Koma Zebuli ananena naye, Uona mthunzi wa mapiri ndi kuyesa anthu.

37. Koma Gaala ananenanso, nati, Tapenya alikutsika anthu pakati pa dziko, ndi gulu limodzi lidzera olira ya ku thundu wa alauli.

38. Pamenepo Zebuli anati kwa iye, Pakamwa pako mpoti tsopano, muja udanena, Ndani Abimeleki kud timtumikire? awa si anthuwo unawapeputsa? uturuke tsopano, nulimbane nao.

39. Ndipo Gaala anaturuka pamaso pao pa eni ace a ku Sekemu, nalimbana ndi Abimeleki.

40. Koma Abimeleki anampitikitsa, nathawa iye pamaso pace; nagwa olasidwa ambiri mpaka polowera pa cipata.

41. Ndipo Abimeleki anakhala ku Aruma; ndi Zebuli anafngitsa Gaala ndi abale ace kuti asakhale m'Sekemu.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 9