Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 9:28-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Pamenepo Gaala, mwana wa Ebedi anati, Abimeleki ndani, ndi Sekemu ndani, kuti timtumikire? sindiye mwana wa Yerubaala kodi? ndi Zebuli kazembe wace? Mutumikire amuna a Hamori atate wa Sekemu; koma ameneyo timtumikire cifukwa ninji?

29. Mwenzi anthu awa akadakhala m'dzanja langa; ndikadamcotsadi Abimeleki. Ndipo anati kwa Abimeleki, Curukitsa khamu lako, nuturuke.

30. Pamene Zebuli woyang'anira mudzi anamva mau a Gaala mwana wa Ebedi, anapsa mtima.

31. Natuma mithenga kwa Abimeleki monyenga nati, Taonani Gaala ndi abale ace afika ku Sekemu; ndipo taonani, akupandukitsirani mudzi.

32. Ndipo tsopano, taukani usiku, inu ndi anthu okhala nanu ndi kulalira kuthengo;

33. ndipo kukhale kuti m'mawa, pakuturuka dzuwa, muuke mamawa mugwere mudziwo; ndipo taonani, akakuturukirani iye ndi anthu ali naye, uzimcitira monga lidziwa dzanja lako.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 9