Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 4:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo anauza Sisera kuti Baraki mwana wa Abinoamu wakwera ku phiri la Tabori.

13. Pamenepo Sisera anasonkhanitsa magareta ace onse ndiwo magareta mazana asanu ndi anai acitsulo, ndi anthu onse okhala naye, kuyambira Haroseti wa amitundu mpaka mtsinje wa Kisoni.

14. Ndipo Debora anati kwa Baraki, Nyamuka; pakuti ili ndi tsikuli Yehova wapereka Sisera m'dzanja lako; sanaturuka kodi Yehova pamaso pako? Potero Baraki anatsika ku phiri la Tabori ndi amuna zikwi khumi akumtsata.

15. Ndipo Ambuye anaononga Sisera, ndi magareta onse ndi gulu lankhondo lonse, adi lupanga lakuthwa pamaso pa Baraki; koma Sisera anatsika pagareta nathawa coyenda pansi.

16. Koma Baraki anatsata magareta ndi gululo mpaka Haroseti wa amitundu; ndi gulu lonse lankhondo la Sisera linagwa ndi lupanga lakuthwa, sanatsala munthu ndi mmodzi yense.

17. Koma Sisera anathawira coyenda pansi ku hema wa Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; pakuti panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori, ndi nyumba ya Heberi Mkeni.

18. Ndipo Yaeli anaturuka kukomana ndi Sisera, nanena naye, Pambuka, mbuye wanga, pambukira kwa ine kuno; usaope. Ndipo anapambukira kwa iye kulowa m'hema, nampfunda ndi cimbwi.

19. Pamenepo ananena naye, Ndipatsetu madzi pang'ono ndimwe; popeza ndine waludzu. Ndipo anatsegula thumba la mkaka, nampatsa amwe, nampfunda.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 4