Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 3:9-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anaukitsira ana a Israyeli mpulumutsi amene anawapulumutsa, ndiye Otiniyeli mwana wa'Kenazi, mng'ono wace wa Kalebe.

10. Ndipo unamdzera mzimu wa Yehova, iye naweruza Israyeli, naturuka kunkhondo; napereka Yehova Kusani-Risataimu mfumu ya Mesapotamiya m'dzanja lace; ndi dzanja lace linamlaka Kusani-Risataimu.

11. Pamenepo dziko linapumula zaka makumi anai; ndi Otiniveli mwana wa Kenazi anafa.

12. Koma ana a Israyeli anaonjezanso kucita coipa pamaso pa Yehova; pamenepo Yehova analimbitsa Egiloni mfumu ya Moabu pa Israyeli, popeza anacita coipa pamaso pa Yehova.

13. Ndipo anadzisonkanitsira ana a Amoni ndi a Amaleki, namuka nakantha Israyeli, nalanda mudzi wa m'migwalangwa nakhalamo.

14. Ndipo ana a Israyeli anatumildra Egiloni mfumu ya Moabu zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

15. Koma pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anawaukitsira mpulumutsi, Ehudi mwana wa Gera, Mbenjamini, munthu wamanzere, ndipo ana a Israyeli anatumiza mtulo m'dzanja lace Ikwa Egiloni mfumu ya Moabu.

16. Ndipo Ehudi anadzisulira lupanga lakuthwa konse konse utali wace mkono; nalimangirira pansi pa zobvala zace pa ncafu ya kulamanja.

17. Ndipo anapereka mtulo kwa Egiloni, mfumu ya Moabu; koma Egiloni ndiye munthu wonenepa ndithu.

18. Ndipo atatha kupereka mtulowo, anauza anthu onyamula mtulo acoke.

19. Koma iye mwini anabwerera pa mafano osema ali ku Giligala, nati, Ndiri nao mau acinsinsi kwa inu, mfumu. Nati iye, Khalani cete. Ndipo anaturuka onse akuimapo.

20. Ndipo Ehudi anamdzera alikukhala pa yekha m'cipinda cosanja copitidwa mphepo, Nati Ehudi, Ndiri nao mau a Mulungu akukuuzani. Nauka iye pa mpando wace.

21. Ndipo Ehudi anaturutsa dzanja lace lamanzere nagwira lupanga ku ncafu ya kulamanja nampyoza m'mimba mwace;

22. ndi cigumbu cace cinalowa kutsata mpeni wace; ndi mafuta anaphimba mpeniwo, pakuti sanasolola lupanga m'mimba mwace; nilituruka kumbuyo.

23. Pamenepo Ehudi anaturuka kukhonde namtsekera pamakomo pa cipinda cosanja nafungulira.

24. Ndipo ataturuka iye, anadza aka polo ace; napenya, ndipo taonani pamakomo pa cipinda cosanja mpofungulira; nati iwo, Angophimba mapazi m'cipinda cace cosanja copitidwa mphepo.

25. Ndipo analindirira mpaka anacita manyazi; koma taonani, sanatsegula pamakomo pa cipinda cosanja. Pamenepo anatenga mfungulo natsegula; ndipo taonani, mbuye wao wagwa pansi, wafa.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 3