Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 21:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo analamulira ana a Benjamini ndi kuti, Mukani, mulalire m'minda yamphesa;

21. nimuyang'ane, ndipo taonani, ataturuka ana akazi a Silo kubvinabvina, pamenepo muturuke m'minda yamphesa ndi kudzigwirira yense mkazi wace mwa ana akazi a Silo, ndi kumuka naye ku dziko la Benjamini.

22. Ndipo kudzali, akatifikira atate ao kapena alongo ao kunena nafe mlandu, tidzanena nao, Mutipatse awa, pakuti sitinawatengera yense mkazi wace kunkhondo; pakuti inunso simunawaninkha awa; mukadatero mukadaparamula tsopano.

23. Nacita cotere ana a Benjamini, nadzitengera akazi monga mwa kuwerenga kwao, a obvina aja, amene anawatenga mwacifwamba; namuka iwo nabwerera ku colowa cao, namanga midzi, nakhalamo.

24. Ndipo ana a Israyeli anacokako nthawi ija yense kumka ku pfuko lace, ndi banja lace, naturukako yense kumka ku colowa cace.

25. Panalibe mfumu m'Israyeli masiku aja; a yense anacita comkomera pamaso pace.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 21