18. Koma sitikhoza ife kuwapatsa ana athu akazi akhale akazi ao; pakuti ana a Israyeli adalumbira ndi kuti, Atembereredwe wakupatsa Abenjamini mkazi.
19. Natiiwo, Taonani, pali madyerero a Yehova caka ndi caka ku Silo, ndiko kumpoto kwa Beteli, kum'mawa kwa mseu wokwera kucokera ku Beteli kumka ku Sekemu, ndi kumwela kwa Lebona.
20. Ndipo analamulira ana a Benjamini ndi kuti, Mukani, mulalire m'minda yamphesa;
21. nimuyang'ane, ndipo taonani, ataturuka ana akazi a Silo kubvinabvina, pamenepo muturuke m'minda yamphesa ndi kudzigwirira yense mkazi wace mwa ana akazi a Silo, ndi kumuka naye ku dziko la Benjamini.
22. Ndipo kudzali, akatifikira atate ao kapena alongo ao kunena nafe mlandu, tidzanena nao, Mutipatse awa, pakuti sitinawatengera yense mkazi wace kunkhondo; pakuti inunso simunawaninkha awa; mukadatero mukadaparamula tsopano.