Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 18:18-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Atalowa iwo m'nyumba ya Mika, natengako fane losema, cobvala ca wansembe, ndi timafano, ndi fano loyenga, wansembeyo ananena nao, Mucitanji?

19. Ndipo ananena naye, Khala cete, tseka pakamwa pako, numuke nafe, nutikhalire atate ndi wansembe wathu; cikukomera nciti, kukhala wansembe wa nyumba ya munthu mmodzi, kapena kukhala wansembe wa pfuko ndi banja m'Israyeli?

20. Nukondwera mtima wa wansembeyo, natenga iye cobvala ca wansembe, ndi timafano ndi fano losema, nalowa pakati pa anthu.

21. Atatero anabwerera, nacoka, natsogoza ana ang'ono ndi zoweta ndi akatundu.

22. Atafika kutari ndi nyumba ya Mika, Mikayo anawamemeza amuna a m'nyumba zoyandikizana ndi yace, natsata ndi kuwapeza ana a Dani.

23. Ndipo anapfuula kwa ana a Dani. Naceuka iwo nati kwa Mika, Cakusowa ciani, kuti wamemeza anthu ako?

24. Nati iye, Mwanditengera milungu yanga ndinaipanga, ndi wansembe, ndi kucoka; cinditsaliranso ciani? ndipo muneneranji kwa ine, Cakusowa nciani?

25. Koma ana a Dani anati kwa iye, Mau ako asamveke ndi ife, angakugwere anthu owawa mtima, nukataya moyo wako ndi wa iwo a m'nyumba mwako.

26. Nayenda ulendo wao ana a Dani; ndipo Mika pakuona kuti anamposa mphamvu, anatembenuka nabwerera kunyumba kwace.

27. M'mwemo anatenga zimene Mika adacipanga, ndi wansembe anali naye, nafika ku Laisi, kwa anthu odekha ndi okhazikika mtima, nawakantha ndi lupanga lakuthwa, natentha mudzi wao ndi moto.

28. Ndipo panalibe wolanditsa, popeza ku Sidoni nkutali, ndipo analibe kuyenderana ndi anthu ena; ndiko ku cigwa cokhala ku Betirehobo. Pamenepo anamanganso mudziwo, nakhala m'mwemo.

29. Ndipo analicha dzina la mudziwo Dani, kutsata dzina la atate wao Dani wombala Israyeli; koma poyambapo dzina la mudzi linali Laisi.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 18