Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 18:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Masiku ajawo panalibe mfumu m'Israyeli; masiku ajanso pfuko la Adani anadzifunira colowa cakukhalako; pakuti kufikira tsiku lija sicinawagwera colowa cao pakati pa mapfuko a Israyeli.

2. Ndipo ana a Dani anatuma a banja lao amuna asanu a mwa iwo onse, anthu olimba mtima, a ku Zora, ndi a ku Esitaoli, a kuzonda dziko ndi kufunafunamo; nanena nao, Mukani, mufunefune m'dziko. Nafika iwo ku mapiri a Efraimu ku nyumba ya Mika, nagona komweko,

3. Pokhala iwo m'nyumba ya Mika, anazindikira mau a mnyamata Mleviyo, napambukirako, nanena naye, Anadza nawe kuno ndani? ucitanji muno? ukhala naco ciani kuno?

4. Ndipo ananena nao, Mika anandicitira cakuti cakuti, napangana nane za nchito, ndipo ndikhala wansembe wace.

5. Pamenepo ananena naye, Utifunsire kwa Mulungu, kuti tidziwe ngati ulendo wathu timukawo udzakoma.

6. Nanena nao wansembeyo, Mukani mumtendere, ulendo wanu muyendawo uli pamaso pa Yehova.

7. Pamenepo amuna asanuwa anacoka, nafika ku Laisi; naona anthu anali m'mwemo, kuti anakhalaokhazikika mtima, monga anakhala Asidoni, odekha ndi osatekeseka; popeza m'dzikomo munalibe mwini bwalo wakudtitsa manyazi m'cinthu ciri conse; nasiyana kutali ndi Asidoni, ndipo analibe kanthu ndi munthu ali yense.

8. Ndipo asanuwo anafikanso kwa abale ao ku Zora ndi Esitaoli; ndi abale ao ananena nao, Mutani inu?

9. Nati iwo, Taukani, tiwakwerere; pakuti tapenya dziko, ndipo taonani, ndilo lokoma ndithu; ndi inu muli cete kodi? musamacita ulesi kumuka ndi kulowa kulandira dzikolo,

10. Pomuka inu mudzafikira anthu okhazikika mtima ndi dziko ladtando; pakuti Mulungu walipereka m'dzanja lanu; pamenepo mposasowa kanthu kali konse kali pa dziko lapansi.

11. Pamenepo amuna mazana asanu ndi limodzi, omangira zida za nkhondo m'cuuno, anaphumulako a banja la a Dani, anacokera ku Zora, ndi ku Esitaoli.

12. Nakwera namanga misasa m'Kiriyati-yearimu, m'Yuda; cifukwa cace anacha dzina lace la malowo cigono ca Dani, mpaka lero; taona, ali m'tseri mwa Kiriyatiyearimu.

13. Ndipo anapiririra komweko kumka ku mapiri a Efraimu, nadza ku nyumba ya Mika.

14. Pamenepo anayankha amuna asanu anamukawo kukazonda dziko la Laisi, nanena ndi abale ao, Kodi mudziwa kuti m'nyumba izi muli cobvala ca wansembe, ndi timafano ndi fano losema, ndi fano loyenga? Ndipo tsopano dziwani coyenera inu kucita.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 18