17. Pomwepo anamfotokozera mtima wace wonse, nanena naye, Pamutu panga sipanapite lumo, pakuti ndine Mnaziri wa Mulungu ciyambire mimba ya mai wanga; akandimeta, mphamvu yanga idzandicokera, ndidzakhala wofoka wakunga munthu wina ali yense.
18. Ndipo pamene Delila anaona kuti adamfotokozera mtima wace wonse, anatuma naitana akalonga a Afilisti, ndi kuti, Kwerani nthawi yino, pakuti wandifotokozera za mtima wace wonse. Nakwera akalonga a Afilisti nadza kwa iye nabwera nazo ndalamazo m'dzanja lao.
19. Pamenepo anamgonetsa pa mabondo ace, naitana munthu, nameta njombi zace zisanu ndi ziwiri; nayamba kumzunza, nimcokera mphamvu yaceo
20. Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samsoni. Nagalamuka iye m'tulo tace, nati, Ndizituruka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwa kuti Yehova adamcokera.