Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 1:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anapeza Adoni-bezeki m'Bezeki, namthira nkhondo nakantha Akanani ndi Aperizi.

6. Koma Adoni-bezeki anathawa; ndipo anampitikitsa, namgwira, namdula zala zazikuru za m'manja ndi za m'mapazi.

7. Pamenepo anati Adoni-bezeki, Mafumu makumi asanu ndi awiri odulidwa zala zazikuru za m'manja ndi m'mapazi anaola kakudya kao pansi pa gome panga; monga ndinacita ine, momwemo Mulungu wandibwezera. Ndipo anadza naye ku Yerusalemu, nafa iye komweko.

8. Ndipo ana a Yuda anacita nkhondo pa Yerusalemu, naulanda, naukantha ndi lupanga lakuthwa, natentha mudzi ndi moto.

9. Ndipo atatero ana a Yuda anatsika kuthirana nao nkhondo Akanani akukhala kumapiri, ndi kumwela ndi kucidikha.

10. Ndipo Yuda anamuka kwa Akanani akukhala m'Hebroni; koma kale dzina la Hebroni ndilo mudzi wa Ariba; ndipo anakantha Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai.

11. Pocoka pamenepo anamuka kwa nzika za ku Dibiri, koma kale dzina la Dibiri ndilo mudzi wa Seferi.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 1