Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 1:34-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo Aamori anakankha ana a Dani akhale kumapiri pakuti sanawalola atsikire kucigwa;

35. Aamori anakhumbanso kukhala ku phiri la Heresi, ku Ajaloni, ndi ku Saalibimu; koma dzanja la a m'nyumba ya Yosefe linawalaka, nakhala iwo akupereka msonkho.

36. Ndipo malire a Aamori anayambira pokwerera pa Akrabimu, pathanthwe, ndi pokwererapo.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 1